Mutu 18

1 Pamene vinasila ivi Paulo anacoka mu Athenzi noyenda ku Korinto. 2 Kuja anapeza mu Yuda winangu zina lake ni Akwila, mwamuna waku Pontasi pamutundu; enza anacoka ku Itali camanje manje pamozi namukazi wake Prisila, cifukwa Kilaudi analamulila kuti bonse Ayuda acoke mu Romu; ndipo Paulo anabwela kwa beve; 3 Paulo anankhala nabeve cifukwa benzo cita malando yasemu. Benzo panga matenti. 4 So Paulo anakambilana mu sinagoge Sabata iliyonse. Anasimikizila Ayuda naba Giliki. 5 Koma pamene Sailasi na Timoti anabwela kucoka ku Mesedoniya, Paulo anauziwa na Mzimu kuti apeleke umboni kui Ayuda kuti Yesu ndiye Kristu. 6 Pamene Ayuda banamususha nomunyoza, Paulo anakunkhumula malaya yake kuli beve nokamba ati, "Lekani mwazi wanu unkhale pamitu wanu; Ine nilibe mulandu. Kucokela lero nizayenda kwa akunja." 7 Pamene apo anacoka noyenda kunyumba ya Titiyasi Jasitasi, mwamuna enzo lambila Mulungu. Nyumba yake yenze pafupi na Sinagoge. 8 Khirisipasi, msogoleli wa sinagoge nanyumba yake yonse anakhulupila mwa Ambuye. Bambila baku Korinto bamene anamvela Paulo anakhulupilila nobatizika. 9 Ambuye anakamba ati kwa Paulo usiku mumaso mphenya, Usayope, kamba ndipo usankhale cete. 10 Cifukwa nilinaiwe, ndipo kulibe azayesa kukucita ngozi, cifukwa ninabanthu bambili mu tauni iyi." 11 Paulo anankhalamo caka cimozi na myezi ili 6, kuphunzisa mau ya Mulungu pakati pawo. 12 Koma pamene Galiyo anankhala govana wakuAkaya, Ayuda bonse pamozi anaukila Paulo nomuleta pamupando waciweluzo, 13 nokamba ati, "Uyu mwamuna akoka banthu luti alambile Mulungu mosushana nalamulo." 14 Ndipo pamene Paulo enzo funa kukamba, Galiyo anakamba ati kuli ba Yuda, "Imwe Ayuda, ngati yenzeli nkhani ya cinthu coipa or mulandu, sembe cezebwino kuku diling'ani. 15 Koma cifukwa cakuti aya nimafunso pa mau nama zina nalamulo yanu, kambilanani. Sinifuna kunkhala oweluza pali izi nkhani." 16 Galiyo anabacosa pamupando oweluzila. 17 so bonse banagwila Sosithenesi, olamulila sinagoge, nomumenya pasogolo pamupando oweluzila. Koma Galiyo sanafakileko nzeru pavamene anacita. 18 Paulo ponkhalako masiku yambili, anabasiya abale noyenda ku Siliya pamozi na Prisila na Akwila. Akalibe ucoka pokwelela boti, Kensiriya anagelewa mumutu wake cifukwa enze anapanga pagano yamu Nazareti. 19 Pamene anafika kwa Aifenso, Paulo anasiya Prisila na Akwila kuja, koma iye anayenda mu sinagoge nokambilana na Ayuda. 20 Pamene banapempha Paulo kuti ankhaleko nthawi itali, anakana. 21 Koma pocokapo pali beve, anakamba ati, "Nizabwela futi kwa imwe ngati nicifuniro ca Mulungu." Anabwela acoka kwa Aifenso. 22 Pamene Paulo anafika ku Sizariya, anayenda kupasa moni mupingo waku Yelusalemu nobwelo yenda ku Antioku. 23 Pamene anakhalako pakanthawi, Paulo anacoka nopitila kumizinda ya Galatiya na Friyiya nolimbika ophunzila bonse. 24 Manje mu Yuda winangu zina lake Apolosi wobadwila ku Alekizanda, anabwela ku Aifenso. Enzo ziba bwino mumakambidwe ndiponso namalemba enzo yaziba bwino. 25 Apolosi anaphunzisiwa muziphunziso za Ambuye. Pakunkhala wa cangu mwa yeve, anaphunzisa bwino zinthu zokhuzana na Yesu, koma enzo ziba cabe ubatizo wa Yohane. 26 Apolosi anayamba kukamba molimbika mu sinagoge. Koma pamene Prisila na Akwila anamumvera, anamupanga muzawo nomufotokozela njila ya Mulungu bwini bwino. 27 Pamene anafuna kupitila ku Akaya, ba bale anamulimbikisa nolembela ophunzila baku Akaya kuti amulandile. Pamene anafika, anathandizila maningi baja bamene anakhulupilila mwa cisomo. 28 Apolosi anagonjesa Ayuda benangu pamenso pabanthu namakambidwe yosusha bwino na ukwaswili wake mumakambidwe; mukuwonesela mwa malemba kuti Yesu enzeli Kristu.