Mutu 1

1 Paulo, Siluvano na Timoti, ku mpingo wa Atesalonika mwa Mulungu ba Tate batu na Ambuye Yesu Kristu. 2 Chisomo na mutendere kuli iwe kuchokela kuli Mulungu ba Tate batu na Ambuye Yesu Kristu. 3 Tiyenela kupeleka mayamiko kuli Mulungu chifukwa cha imwe, abale, chifukwa chikulupililo chanu chikula maningi maningi, na chikondi chamene ali onse mwa imwe ali nacho pali wina na muzake. 4 Chifukwa chake ise tikamba momvela bwino pali imwe mu mipingo zonse za Mulungu chifukwa cha kupilila kwanu na chikulupililo mu kuvutika kwanu konse, na mu kuvutika kwamene mupitamo. 5 Ichi ndiye cho onesa kuweluza kwa chilungamo kwa Mulungu, mwakuti imwe muka tengeko mbali moyenela mu ufumu wa Mulungu, wamene imwe muvutikila. 6 Chifukwa zoona, nicholungama kuti Mulungu abwezele mavuto ku baja bamene bakuvutisani imwe, 7 na ku tontoza baja bamene bavutikila pamozi na ise, pamene Ambuye Yesu Kristu bazaonekeselewa kuchokela kumwamba pamozi na bangelo bake bampavu 8 mu moto oyaka, kubwezela voipa pali baja bamene sibaziba Mulungu napali baja bamene sibamvela mau ya utenga wabwino wa Ambuye Yesu. 9 Bazalangiwa na chionongeko chamuyayaya kuchokapo pa menso pa Ambuye na ulemelelo wa mpavu zao. 10 Bazachita ichi pamene bazabwela kuza lemekezeka mu bantu babo boyela naku lemekezeka kuli baja bokulupilila, chifukwa umboni watu kuli imwe unakululupiliwa. 11 Chifukwa cha ichi naise tipempela imwe mosasiya, kuti Mulungu watu akuganizileni kunkala boyenela kuitaniwa kwanu pamozi na mpavu zao bakwanilise yonse maganizo yabwino na ntchito yonse ya chikululupilo. 12 Tipempela kuti zina ya Ambuye watu Yesu ilemekezewe mwa imwe, na imwe mwa beve, kulingana na chisomo cha Mulungu na Ambuye Yesu Kristu.