Mutu 13

1 Munthu wa Mulungu anachokela ku Yuda na mau ya Yehova anabwela ku Beteli. Yerobowamu anaimilila pafupi na guwa yansembe kuti ashoke lubani. 2 eve analilila pa guwa yansembe mu mau a Yehova kuti: “Guwa yansembe, guwa yansembe! Ivi nde vamane Yehova anakamba, 'Ona, mwana mwamuna zina yake Yosiya azabadwa m'banja ya Davide, ndipo azapeleka nsembe kuli iwe nsembe ya misanje yamene azashokela lubani kuli iwe; pali iwe aza shoka ma bonzo ya ba banthu. 3 Ndipo munthu wa Mulungu anapasa chilangizo siku yamene ija, kukamba, Ichi nichilangizo kuti Yehova akamba: Onani, guwa ya nsembe yagabanikana; ndipo milota yasanduliwa.'" 4 Pamene mfumu ananvela vamene mwana mwamuna wa Mulungu anakamba, kuti analilila guwa yansembe ku Beteli, Yeroboamu anatambulula kwanja yake kuchokela pa guwa, kukamba, “Mgwileni.” kwanja yamene anatambulula mwamuna inayuma, kuti asabwewlele kuli eve. 5 (Guwa yansembe inagabanikana ndipo milota inasanulidwa paguwa, monga kunalongosolela na chilangizo chamene munthu wa Mulungu uja anapleleka mu mau ya Yahweh.) 6 Mfumu Yerobiamu anayanka nakukamba kuli munthu wa Mulungu ati, "Pempa kuti Yehova Mulungu wako ankale nau bwino ndipo unipempelele, kuti kwanja yanga ibwelele kuli ine." Kapolo wa Mulungu anapempela kuli Yehova, ndipo kwanja ya mfumu inabwezewa kuli eve, ndipo chinankala monga poyamba. 7 Mfumu inauza kapolo wa Mulungu uja, "bwela kunyumba naine ukapumule, ndipo nizakupasa mphaso." 8 Kapolo wa Mulungu ana kamba kuli mfumu, "nangu unipase pakati pa chuma chako, sinizayenda naiwe, kapena kudya kapena kumwa manzi pamalo pano, 9 chifukwa Yehova ananilamulila mu mau yake kuti, 'Usadye mukate kapena kumwa manzi, kapena kubwelela panjila yamene wabwelela.” 10 kapolo wa Mulungu leka njila ina ndipo sanabwelele kunyumba kwake kupitila njila yamene anapitila ku Beteli. 11 Manje panali mneneli mukulu wamene ankakala ku Beteli, ndipo umozi mwana wake paba muna anabwela kumu uza vonse vamene kapolo wa Mulungu anachita pa siku ija mu Beteli. bana bake bamuna banamu uza mau yamene kapolo wa Mulungu anakamba kuli mfumu. 12 Ba tate babo banakamba kuli beve, "Anayenda njila iti?" Manje bana bake ba muna banaona njila ya kapolo wa Mulungu yochokela ku Yuda. 13 Ndipo anakamba kuli bana bake bamuna, Nimangileni mbela pa bulu wake. Ndipo anamangilila bulu, naku; ikwela. 14 Mneneli mukulu pa sogolo pa kapolo wa Mulungu anamupeza ankala pansi pa mtengo ikulu; ndipo anakamba kuli eve, Ndiwe kapoo wa Mulungu anachokela ku Yuda? Eve anayanka, "Ndine." 15 Ndipo mneneli mukulu anakamba kuli eve, "Bwelela naine kunyumba ukadye na chakudya." 16 kapolo wa Mulungu anayanka kuti, "Sindingabwelele naiwe kapena kungena naiwe, kapena kudya chakudya kapena kumwa manzi pamozi naiwe pamalo yano, 17 chifukwa aninilamulila Yehova kuti, 'Usadye chakudya kapena kumwa manzi kwamene uko, ndipo musabwelele njila yamene munabwelela.'” 18 Ndipo mneneli mukulu anakamba kuli eve, naine ndine mneneli monga iwe, ndipo mngeli anakamba kuli ine mu mau ya Yehova, kukamba, Mubwele naye kunyumba kwako kuti akadye chakudya na kumwa manzi. '"Koma anali kunama kuli kapolo wa Mulungu. 19 koma kapolo wa Mulungu anabwelela na mneneli mukulu ndipo anakadya chakudya munyumba mwake na kumwa manzi. 20 Pamene banankala pa tebo, mau ya Yehova yanabwela kuli mneneli wamene anamuleta kuli eve, 21 ndipo ana lila kuli kapolo wa Mulungu wamene anabwela kuchokela ku Yuda, kukamba, Yehova akamba, Chifukwa sunamvela mau ya Yehova ndipo simunasunge lamulo yamene Yehova Mulungu wanu anakupasani, 22 koma munabwela na kudya na kumwa manzi kumalo kwamene Yehova anaku uzani kuti musadye kapena kumwa manzi, tupi yanu sizashikiwa m'manda yaba tate bano. 23 Kuchokela kudya na kumwa, mneneli anakwela bulu kapolo wa Mulungu, muntu wamene anabwelela naye. 24 Pamene kapolo wa Mulungu anayenda, nkalamu ina mukumana panjila nakumupaya, ndipo tupi yake inasala panjila. Bulu inaimilia pambali pake, ndipo nkalamu nayeve inaimilia pafupi pa tupi. 25 pamene bamuna bana pita naku ona tupi ina sala panjila, ndipo nkalamu inamilila pafupi na tupi, banabwela naku kamba mu mzinda mwamene mneneli mukulu enzonkala. 26 Pamene mneneli wamene anamubwealesa kuchokela ku njila ija anakamba, "Ni kapolo wa Mulungu wamene sananvele mau ya Yehova. Chifukwa ichi Yehova anamupeleka kuli nkalamu, ndipo ana mujubajuba mutungono naku mu paya, mau ya Yehova anamuchenjeza. " 27 Ndipo mneneli mukulu anakamba na bana bake bamuna, kukamba, "Mangililani bulu yanga," ndipo banaimangilila. 28 Anayenda nakapeza tupi inasala panjila, bulu na nkalamu kuimilila pafupi na tupi. Nkalamu sinadye chitumbi kapena ku gonjesa bulu. 29 Pamene mneneli ananyamula chitumbi cha kopolo wa Mulungu, ana chiika pa bulu, naku chibweza. anabwela mzinda kwao kumulila na kumushika m'manda. 30 Anayika chitumbi chake m'manda wake, ndipo banamulia, kuti, "soka, m'bale wanga!" 31 Pamene ana mushika m'manda, mneneli mukulu anakamba anakamba kuli bana bake ba muna, kuti, "Ngati nafa mukanishike m'manda mwamene kapolo wa Mulungu anashikiwa. Ikani mabonzo yanga pafupi nama bonzo yake. 32 Koma uthenga ana kambilila mu mau ya Yehova, kunyamukila guwa ya nsembe mu Beteli, na manyumba yonse yakumalo yokwezeka m'mizinda ya Samariya, viza chitika zoona." 33 kuchoka ichi Yerobiamu sanasiye kuchoka ku njila zake zoipa, koma anapitiliza kusanka bansembe bosayenla kuchokela ku bantu osiyanasiyana. Aliyense wamene anatumikila anali kupatula bansembe. 34 Iyi nkhani inankala chimo ku banja ya Yeroboamu ndipo inachitisa kuti banja yake iwonongeke na kufafaniziwa pa ziko yapansi.